Phunziro losangalatsa komanso lozama ili pa mutu wa “chikhulupiriro” lidzakopa wina aliyense yemwe cholinga chake ndi kukondweretsa Mulungu. Pakuti popanda chikhulupiriro n’zosatheka kukondweretsa Mulungu, malemba amanena choncho.
Ichi ndichifukwa chake bukuli ndilofunika kuwerengedwa ndi aliyense amene ali ndi chikhumbo chokondweretsa Mulungu. Ngati chikhulupiriro chinapangitsa Abrahamu kukhala bwenzi la Mulungu, ndiye kuti chikhulupiriro n’chofunika kwambiri pa kuyenda kwathu ndi Mulungu. Bukuli ndi chuma chenicheni! Dziwani zinsinsi zofunika kuti muyende ndi kukhala ndi moyo mwa chikhulupiriro. Tsegulani zinsinsi za chikhulupiriro zomwe mukuzifunikira kuti muchite zinthu zosatheka m’moyo wanu!

Reviews
There are no reviews yet.