• Popanda kukayika, amene amakonzekera amasiyana kwambiri ndi amene samakonzekera. Kukonzekera ndi kudzikonza bwino pa ntchito yomwe ili patsogolo panu. M’Baibulo lonse timauzidwa kukonzekera zimene zikubwera ndi kudzikonza tokha. Mulungu amazindikira gawo lililonse limene mumatenga kuti muwonetsetse kuti mwakonzeka kukwaniritsa chifuniro chake. Kukonzeka kwanu kutumikira Ambuye kumadalira kukonzekera kwanu! Dziwani kuti ngakhale pokakumana ndi Mulungu tiyenera kukonzekera! M’buku latsopanoli loyembekezeredwa kwa nthawi yaitali, lolembedwa ndi Dag Heward-Mills, mudzatsogoleredwa pa mmene mungakhalire m’moyo wa kukonzeka ndi kukonzekera ntchito zonse zabwino zimene Mulungu wakuyitanani kuti muziwachita! Inu muli pafupi kusiyanitsidwa kudzera m’bukuli!
  • Tikudziwa kui kukula kwa mpingo ndi chinthu chovuta kukwaniritsa. azibusa onse amafuna mpingo wawo ukule. bukhuli ndi yankho la kufuna kwanu kwa kukula kwa mpingo. mukamvetsetsa momwe "zinthu zosiyanasiyana zimawirira pamodzi" kukwaniritsa kukula kwa mpingo. wokondedwa m'busa, pomwe mawu ndi kudzoza kuli m'bukhuli kukubwera mu mtima mwanu, muzakhala ndi kukula kwa mpingo komwe mwakhala mukupempherera.
  • Yesu anagwiritsa ntchito mawu akuti “kulira ndi kukukuta mano” maulendo asanu osiyana m’Baibulo. Ndi chenjezo la uneneri lonena za ululu, mkwiyo, chisoni, kunong’oneza bondo, chikumbumtima, ndi malingaliro a kutayika omwe adzamvedwe pa kulowa kumwamba opanda kukhala wokonzekera uko. Wolemba mabuku wotchuka, Dag Heward-Mills m’njira yake yachizolowezi yosakayikitsa, akufotokoza chowonadi chochititsa mantha cha anthu angati amene adzanong’oneze bondo chifukwa cha kutaya mwayi ali padziko lapansi. Inu muyenera kuchita chilichonse chimene mungathe kuti mupewe kukhala m’gulu la anthu amene adzalira ndi kukukuta mano awo m’kunong’oneza.
  • Kodi zauzimu zidakalipo lero? Nditha kuchitira muuzimu? Ngati Mulungu akadachizabe anthu, chifukwa chani sachiza ali yense? Pezani mayankho ku mafunso amenewa ndi ena ambiri a zionetsero za Mzimu Woyera kudzera mu masamba a bukhu losangalatsali lolembedwa ndi Dag Heward-Mills.
  • Kuti mutumikire Mulungu, anthu amachita zinthu zosiyanasiyana.  Ena amapita kusukulu za Baibulo, ena amapita kusukulu zadziko, ena amapereka zopereka kwa anthu a Mulungu ndipo ena amapemphera ndi kusala kudya.  Komabe, palibe chilichonse mwazinthu izi ndi chofanana ndi luso lofunikira lakuwona ndi kumva.  Kuwona ndi kumva, ndiko kugwiritsa ntchito chidziwitso chomwe mwalandira.  Kuwona ndi kumva, ndi njira yeniyeni yolandirira zambiri za Mulungu m'moyo wanu. Mu bukhu lozindikiritsa kwambiri ili, lolembedwa ndi abusa, mphunzitsi, ndi wolemba wochita bwino, Dag Heward-Mills, akugawana zinthu zomwe waziwona ndi kuzimva.  Amauza ena zinthu zomwe wakumana nazo.  Iye amatiphunzitsa mmene tingapezere nzeru za kuona ndi kumva.  Kodi mukufuna kukhala mwana wanzeru wodzipereka ku luso lakuwona ndi kumva? Ndiye bukhu ili ndi lanu!
  • Kudzoza ndi chifungulo chachichikulu chofunikira kutsegula khomo la kuchita bwino ndo kukwaniritsa utumiki. Anthu ambiri ayesera kuchita ntchito ya Mulungu chifukwa cha mafuno abwino, popanda kufika kutali analephera kuzindikira kuti “Ndi khamu la nkhondo ai, ndi mphamvu ai, koma ndi Mzimu Wanga (Kudzoza)” [Zekariya 4:4]. Bukhu lapderali “Kupeza Kudzoza” lolembedwa ndi Bishopu Dag Heward-mills lizakuphunzitsani inu zomwe zimatanthauza kupeza kudzoza ndi momwe mungapangire! Lolani chikhumbo khumbo cha Kudzoza kwa Mulungu kutakasike mkati mwanu kudzera mu masamba a m’bukhuli!
  • Kusabereka ndi chifukwa chosowa zipatso zenizeni mu mpingo wachiKhristu wamakono. Pali ntchito zambiri komanso mapulogalamu ambiri koma pali zipatso zochepa kapena palibe. Pali zambiri ku utumiki kuposa kupeza ziphaso zambiri za chidziwitso cha Baibulo. Abusa ambiri amagwa mu ulendo wawo chifukwa chokhumudwa komanso kunyengedwa chifukwa chakuti ndi osabala mu utumiki. Mulungu amafuna kuti tizibala zipatso. Mulungu akufuna kuti tiwonjezekere mu utumiki. Kuti mubereke muyenera kumvetsetsa kuti kusabereka kumatanthauza chiyani. Kusabereka ndi vuto lomwe Mulungu akufuna kuthana nalo mu utumiki wanu. Bukhu lapanthawi yake limeneli, lolembedwa ndi Dag Heward-Mills lidzakuthandizani kuleka kusabereka mu utumiki wanu. Mzimu wosabereka ukachotsedwa mudzayamba kubala zipatso. Mukutuluka mu kusabereka lero!
  • Azibusa ali pa mpani pani wokondweretsa ndi kusangalatsa anthu awo ndi uthenga wabwino. Mpani pani wa anthu umenewu wapangitsa kusintha kwa mawu a Khristu kufikira mawu a mtanda akhalira kovuta kuzindikirika. Lero, tikubwerera ku maziko a chilungamo cha Chikhristu choti tikuyenera “kutaya” kuti “tipeze” Khristu. Mphamvu izabwerera ku mpingo pamene tikulalikira kuti tipereke nsembe, kusautsidwa ndi kufa chifukwa cha Khristu. Mphamvu ya mawu a Khristu siingafufutidwe ndi wina aliyense posatengera kuchita bwino kapena kukhala wa mphamvu.
  • Mayankho ochitika ku zovuta za kayendetsedwe ka mpingo akuwonetsedweratu mu bukhu la pamwamba latsopanoli la Dag Heward-Mills
  • Nkovuta kupangitsa munthu kumwa chakumwa ngati alibe ludzu. Ndi njala komanso ludzu la Mulugu lokha zitha kukuikani pa ulendo wozama. Kodi mukufuna kusangalala ndi zinthu zozama za Mulungu? Ndine wotsimikiza kuti mukufuna ndicho chifukwa chake mukuwerenga bukhuli. Kumbukirani, “Odala ali akumva njala ndi ludzu la chilungamo; chifukwa adzakhuta”. Mukadzadzidwe pamene mukuzama ndi kuchita zambiri!
  • Mawu a Chigiriki akuti LAIKOS akutanthauza “kupanda luso”. Mbiri yatiphunzitsa kwa nthawi ndi nthawi kuti zinthu zazikulu zakwaniritsidwa kudzera kwa anthu amene “anasowekera luso”. Phunzirani, kudzera mu bukhu lapamwambali lolembedwa ndi Dag Heward-Mills, zomwe zimachitika pamene palibe anthu a wamba kugwira ntchito mu tchalitchi; momwe mungagawanirane zolemetsa ndi anthu wamba ndi momwe tikuyenera kulimbanira kuteteza utumiki wa wamba.
  • Palibe mutu wofunikira kwambiri kuposa kukhala mu chifuniro cha Mulungu. Chokhacho chomwe chikasiyanitse azitumiki a uthenga ndi kuthekera kwawo kwa kumva mawu a Mulungu molondola. Momwe kulili kwabwino kutsatira Mzimu Woyera ku chifuniro cha Mulungu. Mukakhala mu chifuniro cha Mulungu, muzachita bwino ndipo muzakwaniritsa zokhumba zonse kwa Mulungu. Ntchito yapamwambayi yolembedwa ndi Dag Heward-Mills izakhala ndi kukhudza kwakukulu pa moyo wanu ndi utumiki.

Title

Go to Top