Dag Heward-Mills ndi wolemba wa mabuku ambiri, kuphatikizapo logulitsidwa kwambiri “Kukhulupirika ndi Kusakhulupirika”. Ndi woyambitsa wa Mipingo ingapo yochokera ku Lighthose ndi matchalitchi zikwi zitatu.
Dag Heward-Mills, mvangeli wadziko lonse, amatumikira mu misonkhano ya machiritso mu maiko komanso misonkhano ya atsogoleri padziko lonse. Kuti mudziwe zambiri, pitani pa
www.daghewardmills.org.

  • Mu bukhu lapamwambali, Dag Heward-Mills akupereka kuzindikira kwakukulu kwa zochitika m'banja. Bukhu lodabwitsali likagwira ntchito ngati chipangizo chokonzekera kwa phungu wa banja ndi anthu okwatira. Inu mukapeza mu bukhuli, mfundo zotsitsimutsa ndi zosangalatsa zopititsa patsogolo banja lanu. "Bukhu ili ndilodzadza ndi nkhani pa maziko ndi zochitika pa maubwenzi a umunthu mu nthawi imene musanakwatire, muli m'banja ndi ngakhale utatha ukwati. Ili ndi zipangizo zofufuzidwa bwino ndi zovomerezeka pa thunthu ndi kakhalidwe kazolengedwa pazogonana, kubereka kwa anthu, mimba ndi nthawi yobereka ikadutsa. Kuthekera kwa Dotolo Dag Heward-Mills kusintha nkhani zovuta kukhala zophweka ndiye chikhalidwe chosiyanitsa pa bukhuli. Zonse pamodzi, izi zimalipangitsa kukhala bukhu losindikizika lomveka kwambiri, logwiritsika ntchito bwino pa zabanja lero." David Asomani, katswiri wowona za chiberekero cha azimayi. "Bukhu la Bishopu Dag Heward-Mills pa uphungu wa m'banja ndilosowa chifanizo. Maziko ake ngati dotolo wa zachipatala zawonetsedwa momveka bwino mu tsatanetsatane, koma kudzifotokozera kwa zizindikiro zachipatala zomwe zikupangitsa bukhuli kukhala lapadera." Edwin Morgan Ogoe, Mphunzitsi, Sukulu Yaukachenjede ya Ghana, Sukulu Yazachipatala
     
  • Baibulo limatiuza kuti tonse timalakwitsa- Abusa nawo amalakwitsanso. Kulakwitsa kumabwezeretsa m’mbuyo. Kulakwitsa kumalepheretsa kupita chitsogolo. Kodi ndi zolakwitsa ziti zimene abusa anu apanga? Kodi ndi chiyani chingakhale zolakwitsa zazikulu khumi zimene abusa amachita? Muli omasuka kuwerenga Bukuli ndi kuzindikira zolakwika zimene mungazichite ndi m'mene mungazipewere. Buku lofunikali lidzakhala mdalitso kwa inu ndi utumiki wanu.
  • Dr. Dag Heward-Mills, mtsogoleri wa Chikhristu wopambana, akuonetsa chimodzi mwa zinsinsi zake. “Ngati wina atandifunsa chomwe chinsinsi changa chachikulu cha ubale wanga ndi Mulungu chiri, nditha kunena, musaopa, kuti ndi mphamvu ya nthawi za chete yomwe ndimakhala nayo ndi Iye tsiku ndi tsiku.” Iwe waganiza kulemba bukhuli kuti inunso mukapindule kuchokera ku mphamvu ya nthawi ya chete.
  • Anthu ambiri amavutika ndi lingaliro la kupereka chakhumi ingakhale mchitidwe wakale kalewu wabweretsa chuma kwa Ayuda. Mu bukhuli, Bishopu Dag Heward-Mills akuphunzitsa momwe kupereka chakhumi kumapezera mfundo zikulu zikulu za kupanga chuma ndi zozwizitsa za kuchita bwino. Sangalalani ndi limodzi mwa makope a Dag Heward-Mills.
  • Mutu wa bukhuli likukupangitsani kuganiza pompopompo za ana ang'ono akuyimba mokondwa…Mumawerenga Baibulo lanu tsiku lililonse? Mumapemphera tsiku lililonse?Bukhu ili litsekula maso anu ku bukhu lodabwitsa lapalokha lotchedwa Baibulo. Likutsekuliraninso zozizwa zomwe zimadza kwa inu tsiku lililonse pamene mukuwerenga Baibulo ndi kupemphera tsiku lililonse. Kuwerenga Baibulo ndi kupemphera kwanu kwa tsiku lililonse kukhale kosangalasa kwa inu!
  • Kodi zauzimu zidakalipo lero? Nditha kuchitira muuzimu? Ngati Mulungu akadachizabe anthu, chifukwa chani sachiza ali yense? Pezani mayankho ku mafunso amenewa ndi ena ambiri a zionetsero za Mzimu Woyera kudzera mu masamba a bukhu losangalatsali lolembedwa ndi Dag Heward-Mills.
  • Bukhuli ndi chiongolero chapadera ku kumvetsetsa chipulumutso kudzera mwa Yesu Khristu. Mu bukhu la pamwambali, muzamvetsetsa momwe Yesu amakukonderani inu, momwe mungabadwire mwatsopano, momwe mungapewere kupita ku gehena ndi chomwe chimatanthauza kukhala cholengedwa chatsopano mwa Khristu. Perekani bukhuli kwa wina aliyense ndipo azamvetsetsa zomwe zikutanthauza kupulumutsidwa kudzera mu mwazi wa Yesu Khristu.
  • Kodi mukudziwa kuti aneneri akale, anafunsa ndi kufufuza zachipulumutso chachikuluchi chomwe chawonetseredwa kwa ife? Iwo sakanaganiza za momwe chipulumutsochi chingabwerere kwa anthu…koma ndife odalitsika kulandira chipulumutsochi! Ife talandira chipulumutso chifukwa winawake adatiuza za ichi. M'bukhu lopatsa chidwili, Mlaliki Dag Heward-Mills akutitsogolera ife kuti tisangomvetsetsa chipulumutso chathu chachikulu komanso mmene tingagawire ena uthenga wabwino wa chipulumutso chachikuluchi. Aliyense mwaife akachite ntchito ya mlaliki!
  • Pamene muyenda mmoyo inu mukapeza kuti dziko lobisika ndi dziko lenileni ndipo dziko lakuthupi ndi chiwonetsero cha zina mwa zinthu zamu dziko lobisika. Monga mmene mulili ndi adani owoneka, inu mulinso ndi adani obisika. Kodi mungamenyane ndi mdani osamudziwa iye, ndondomeko zake, kapangidwe kake ka zinthu ndi zida zake? Bukhu ili ndi chida chofunika ku ulendo wa moyo wanu. M'bukhu ili mukaphunzira kuti adani anu obisika ndi ati, mizu yakukhala kwawo, maonekedwe awo ndi momwe mungapambanire nkhondo ndi iwo. Bukhu labwinoli likuthandizeni kugonjetsa adani anu obisika!
     
  • Yesu anati: mukhale ochenjera ngati njoka ndi oona mtima ngati nkhunda. Kodi njoka ndizochenjeradi? Nchifukwa chiyani Yesu angapereke langizo ngati limeneli? Tengani kaulendo mu bukhu lopangitsa chidwiri la Dag Heward-Mills, ndi kuzipezera nzeru zobisika za njoka.
  • Palibe mwaife amene wayika dongosolo lokafika kumwamba opanda kuchita chomwe Mulungu amafuna kuti ife tikachite padziko lapansi. Ayi, olo ndi mmodzi! Ife tikufuna timalize ntchito Mulungu watipatsa ife. Bukhu ili ndilokhudza mmene mungakwanitsire utumiki wanu. Bukhu ili ndi kalondolondo ka momwe ife tingayankhire zochitika zaumulungu mmoyo mwathu - ndicholinga chosafuna kupezeka operewera patsikulo. Mukakwaniritse utumiki wanu ndipo Mulungu akanene kwa inu, "Wachita bwino, kapolo wabwino ndi okhulupirika!"
  • Azibusa ali pa mpani pani wokondweretsa ndi kusangalatsa anthu awo ndi uthenga wabwino. Mpani pani wa anthu umenewu wapangitsa kusintha kwa mawu a Khristu kufikira mawu a mtanda akhalira kovuta kuzindikirika. Lero, tikubwerera ku maziko a chilungamo cha Chikhristu choti tikuyenera “kutaya” kuti “tipeze” Khristu. Mphamvu izabwerera ku mpingo pamene tikulalikira kuti tipereke nsembe, kusautsidwa ndi kufa chifukwa cha Khristu. Mphamvu ya mawu a Khristu siingafufutidwe ndi wina aliyense posatengera kuchita bwino kapena kukhala wa mphamvu.

Title

Go to Top