Dag Heward-Mills ndi wolemba wa mabuku ambiri, kuphatikizapo logulitsidwa kwambiri “Kukhulupirika ndi Kusakhulupirika”. Ndi woyambitsa wa Mipingo ingapo yochokera ku Lighthose ndi matchalitchi zikwi zitatu.
Dag Heward-Mills, mvangeli wadziko lonse, amatumikira mu misonkhano ya machiritso mu maiko komanso misonkhano ya atsogoleri padziko lonse. Kuti mudziwe zambiri, pitani pa
www.daghewardmills.org.
-
Baibulo limatichenjeza mosapita m’mbali kuti zokhumudwitsa zidzafika kwa ife. Izi zikutanthauza kuti padzakhala zochitika m'moyo chomwe sichingakusangalaseni ndikukukhumudwitsani. Kodi chenjezo limeneli limatikonzekeretsa mokwanira kuti tigonjetse pamene takhumudwitsidwa? Kodi mungadzitetezere kuti musakhumudwe? Kodi mudzalola kuti kukhumudwitsa kukupangitseni kusakhulupirika chinthu chamtengo wapatali chotchedwa “kudalira”? Bukhuli ndi bukhu lanu la mayankho ku mafunso owopsa awa. M’bukhu ili, Dag Heward-Mills akufotokoza zotsatira za zolakwa pa ife. Timaphunzira kuti zolakwa zimatipweteka ndi kutikwiyitsa, komanso kuti zolakwa zina zimakhala zovuta kuzikhululukira ndi kuziiwala. Bukhulinso ndi chida chophunzirira momwe tingagonjetsere zolakwa kuti tisakhale akapolo a kukhumudwa. -
Chilichonse chimene Mulungu amanena chimafuna kuleza mtima ndi "Mau a chipiriro changa". Ambiri mwa malonjezano a Mulungu ndi zitsanzo za "Mau a chipiriro changa". Mulungu amalonjeza zinthu zambiri m’Baibulo, koma ambiri mwa malonjezo amenewa amafuna chipiriro kuti akakwaniritsidwe. Kachikenanso, Bishopu Dag Heward-Mills, akufotokoza mosamalitsa m’bukhuli, zokumana nazo za amuna aakulu a m’Baibulo amene anafunika kupirira “Mau a chipiriro changa” kuti akalandire malonjezo a Mulungu. -
…ndipo pomwepo chidzafika chimaliziro. Mateyu 24:14 Ndi chiyani chomwe chingathetse moyo monga mukudziwira? Kodi ndi mphamvu yanji yopangitsa kutha kwa zinthu zonse m'moyo wanu? Kodi chizindikiro cha kutha kwa utumiki wanu padziko lapansi chidzakhala chiyani? Kodi n’chiyani chidzathetse mpingo? Mapeto a chilichonse ndi imfa! Anthu ambiri otchulidwa m’bukhuli anatha momvetsa chisoni. Ndikofunika kudziwa chifukwa chomwe moyo wawo unathera. Ndikofunika kudziwa chifukwa chomwe mautumiki a anthu amathera. Kupyolera mu bukhu lounikirali, mudzaona kuti kudzikuza, kusamvera, chidani, kupotoza, kupanduka ndi kunyoza ndi zina mwa zinthu zosasangalatsa zimene zingawononge moyo wanu ndi utumiki wanu. Utumiki wanu uwomboledwe mathero a m’njira yatsoka mofananamo pamene mulandira nzeru zazikulu kuchokera m’bukhu losonkhezera maganizo limeneli. -
Kuti mutumikire Mulungu, anthu amachita zinthu zosiyanasiyana. Ena amapita kusukulu za Baibulo, ena amapita kusukulu zadziko, ena amapereka zopereka kwa anthu a Mulungu ndipo ena amapemphera ndi kusala kudya. Komabe, palibe chilichonse mwazinthu izi ndi chofanana ndi luso lofunikira lakuwona ndi kumva. Kuwona ndi kumva, ndiko kugwiritsa ntchito chidziwitso chomwe mwalandira. Kuwona ndi kumva, ndi njira yeniyeni yolandirira zambiri za Mulungu m'moyo wanu. Mu bukhu lozindikiritsa kwambiri ili, lolembedwa ndi abusa, mphunzitsi, ndi wolemba wochita bwino, Dag Heward-Mills, akugawana zinthu zomwe waziwona ndi kuzimva. Amauza ena zinthu zomwe wakumana nazo. Iye amatiphunzitsa mmene tingapezere nzeru za kuona ndi kumva. Kodi mukufuna kukhala mwana wanzeru wodzipereka ku luso lakuwona ndi kumva? Ndiye bukhu ili ndi lanu! -
Wophunzira ndi watsopano ku chinachake; iye ndi woyamba. Mulungu si munthu amene wangoikidwa kumene kapena wolengedwa kumene. Palibe chilichonse chokhudza Mulungu chomwe chimamupanga kukhala watsopano. Iye ndiye chiyambi! Mulungu wakhala alipo kuyambira kalekale. Iye ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova wamuyaya. Ndife omwe titha kukhala ongophunzira. Ndife amene timapeza zatsopano tsiku lililonse. Ongophunzira ndi wotseguka ku zoopsa zambiri monga kudzikuza. Ndi kudzikuza kwa munthu amene wangoyamba kumene kumamupangitsa kudzikweza yekha motsutsana ndi maulamuliro omwe akhazikitsidwa kwa zaka zambiri. Lusifara anali wophunzira amene anadzudzulidwa chifukwa cha kudzikuza kwake! Iye anagwa mu “chiweruzo cha mdierekezi”. Kulakwitsa kwakukulu kwa Lusifara kunali kuti analibe kudziyesa koyenera kwa iye mwini mogwirizana ndi Mulungu. Kupyolera m’mitu yochititsa chidwi imeneyi, mulole kuti mutenge ziphunzitso za kudzikuza kwa wophunzira mozama kwambiri, kuopera kuti mungakhale ndi moyo kuti mukwaniritse mfundo iliyonse ya m’bukhu lino kuti mudziwonongere nokha ndi kutsutsidwa. Pulumukani ku ngozi iliyonse ya wongophunzira! -
Yesu anagwiritsa ntchito mawu akuti “kulira ndi kukukuta mano” maulendo asanu osiyana m’Baibulo. Ndi chenjezo la uneneri lonena za ululu, mkwiyo, chisoni, kunong’oneza bondo, chikumbumtima, ndi malingaliro a kutayika omwe adzamvedwe pa kulowa kumwamba opanda kukhala wokonzekera uko. Wolemba mabuku wotchuka, Dag Heward-Mills m’njira yake yachizolowezi yosakayikitsa, akufotokoza chowonadi chochititsa mantha cha anthu angati amene adzanong’oneze bondo chifukwa cha kutaya mwayi ali padziko lapansi. Inu muyenera kuchita chilichonse chimene mungathe kuti mupewe kukhala m’gulu la anthu amene adzalira ndi kukukuta mano awo m’kunong’oneza. -
Pali kusiyana kwakukulu pakati pa kulawa chinachake ndi kutenga nawo gawo. Kulawa chinachake ndiko kuchidya kapena kuchiyesa pa lilime; kutenga nawo gawo ndiko kupitirira kulawa ndi kuzidya. Kabukhu kakang’ono kochititsa chidwi kameneka, kolembedwa ndi Dag Heward-Mills, ndi kokamba za kutumikira Mulungu mopyola mlingo wa munthu wolawa. Mulungu akufuna kuti mutenge nawo zinthu zazikulu zimene wapereka kwa inu mu utumiki. Palibe chifukwa chokhalira olawa pamene mungakhale otenga nawo gawo mu zinthu za Mulungu! -
Nkovuta kupangitsa munthu kumwa chakumwa ngati alibe ludzu. Ndi njala komanso ludzu la Mulugu lokha zitha kukuikani pa ulendo wozama. Kodi mukufuna kusangalala ndi zinthu zozama za Mulungu? Ndine wotsimikiza kuti mukufuna ndicho chifukwa chake mukuwerenga bukhuli. Kumbukirani, “Odala ali akumva njala ndi ludzu la chilungamo; chifukwa adzakhuta”. Mukadzadzidwe pamene mukuzama ndi kuchita zambiri! -
Kukhala wokhulupirika mpaka imfa ndiko kusagonjera moyo wako wonse! Kukhala wokhulupirika mpaka imfa ndiko kukhala wokhulupirika, wokhazikika, wofanana, wosagwedezeka ndi wosasintha kufikira imfa. Pamene mukupitiriza utumiki wanu kwa Ambuye, ndithudi mudzakumana ndi chochitika chopunthwa, kugwa, ndi kusakhulupirika. Yesu akutichenjezanso ku Mateyu 18:7 kuti “…ziyenera kuti zokhumudwitsa zibwere; …” Anthu ambiri amathamanga ndi kufika pamalo pomwe amagwa mwadzidzidzi ndi kugwa pansi pazifukwa zina. Zopunthwitsa zingapangitse kukhala kosatheka kufika mapeto omwe akuyembekezeredwa. Izi ndi zomwe muyenera kupewa! Onetsetsani kuti musagwe pansi ndikutuluka mumpikisanowo. Izi ndi mfundo za Mpulumutsi wathu ndipo ndikofunikira kuti muziwakhulupirira ndikuzichita. Bukhu lapanthawi yake ili lolembedwa ndi wolemba wotchuka Dag Heward-Mills, likulimbikitsani kukhalabe wokhulupirika mpaka kumapeto. -
Aliyense amene sagwiritsa ntchito luso lake lopatsidwa ndi Mulungu pa ufumu, ndi wosabala zipatso ndipo ndi chifaniziro cha mchere umene wataya fungo lake. Yesu anati, kapolo wopanda pake sapindula kanthu. Kodi mulibe phindu mu ufumu? Inu ndinu mchere wa dziko lapansi, kotero muyenera kumveketsa kukhalapo kwanu padziko lapansi lino! Bukhu ili launeneri ndi lopatsa kuganiza mozama za mchere ndi chikoka chake chachinsinsi ndi phindu launeneri ku ufumu wa Mulungu, lidzakupangitsani kulingalira mozama za ubwino wanu kapena kusowa kwake, kwa Mulungu. Muphunzira m’bukhu lovutali tanthauzo la kukhala wopanda pake posanthula ndi kumvetsetsa udindo wa mchere m’miyoyo yathu. OSATI kukhala wabwino pachabe! -
Lonjezo ili pa Yobu 8:7 : “Chingakhale chiyambi chako chinali chaching’ono, koma chimaliziro chako chidzachuluka ndithu” chikutisonyeza kuti Mulungu ali ndi cholinga cha kukula ndi kutukumuka kwa miyoyo yathu. Ndi dalitso lotani nanga kulowetsedwa m’zinsinsi zimene zidzatsogolera ku kukulitsa kwathu! Kupyolera mu zinsinsi zambiri zakukulitsa zovumbulutsidwa ndi wolemba, Dag Heward-Mills, tikuphunzira kuti kukulitsa kudzabwera kwa inu kupyolera mu zowawa, mndandanda wa nkhondo, kupambana ndi kulandira cholowa cha Mulungu. Tikuphunziranso kuti mutha kukulitsidwa mukamagwiritsa ntchito zinsinsi zakukulitsa za kusinkhasinkha, mbiri yakale, mabuku ndi nzeru. Kukulitsa kungathenso kubwera kwa inu kudzera mu nsembe ndi mphamvu zauzimu. Phunzirani zinsinsi zomwe zafotokozedwa m'bukhuli ndi kupindula ndi choonadi chake chodabwitsa.