-
Kutsatira Mulungu ndi ulendo wosangalatsa wopeza zinthu. Kutsatira ndi kutengera anthu ena ndi luso lachikale lophunzirira lomwe Yesu Khristu anasankha ngati njira yaikulu yophunzitsira. M’malo mochita manyazi ndi njira yoyesedwa ndi nthawiyi, ndi nthawi yomvetsetsa kukongola ndi kudzichepetsa kwa luso la kutsatira. Mu bukhuli, muzapeza yemwe, chomwe ndi momwe mungatsatire moyenerera. Bukhu lopambana latsopanoli lolembedwa ndi Dag Heward-Mills lipereka luso la kutsatira malo ake oyenerera mu zokumana zathu za Chikhristu. -
Ngati ndinu m’busa wa nkhosa za Mulungu, muzathandizika kwambiri ndi ntchito yabwinoyi. Masamba amenewa ali ndi malangizo ofotokozedwa bwino, ofunikira pa kuchita bwino kwanu. Bishop Dag Heward-Mills akutenga kuchokera mukukhala kwake kwa zaka zoposera makumi atatu ngati m’busa, kugawana nafe zinthu zochita mu ntchio ya utumiki. Ngati mwasirira kukhala m’busa wa anthu a Mulungu, iri ndi bukhu lokutsogolerani lomwe mwakhala mukulifuna. -
Palibe mwaife amene wayika dongosolo lokafika kumwamba opanda kuchita chomwe Mulungu amafuna kuti ife tikachite padziko lapansi. Ayi, olo ndi mmodzi! Ife tikufuna timalize ntchito Mulungu watipatsa ife. Bukhu ili ndilokhudza mmene mungakwanitsire utumiki wanu. Bukhu ili ndi kalondolondo ka momwe ife tingayankhire zochitika zaumulungu mmoyo mwathu - ndicholinga chosafuna kupezeka operewera patsikulo. Mukakwaniritse utumiki wanu ndipo Mulungu akanene kwa inu, "Wachita bwino, kapolo wabwino ndi okhulupirika!" -
Kodi mukudziwa kuti aneneri akale, anafunsa ndi kufufuza zachipulumutso chachikuluchi chomwe chawonetseredwa kwa ife? Iwo sakanaganiza za momwe chipulumutsochi chingabwerere kwa anthu…koma ndife odalitsika kulandira chipulumutsochi! Ife talandira chipulumutso chifukwa winawake adatiuza za ichi. M'bukhu lopatsa chidwili, Mlaliki Dag Heward-Mills akutitsogolera ife kuti tisangomvetsetsa chipulumutso chathu chachikulu komanso mmene tingagawire ena uthenga wabwino wa chipulumutso chachikuluchi. Aliyense mwaife akachite ntchito ya mlaliki! -
Bukhu latsopanoli, "Malamulo a Ntchito ya Mpingo", ndi chida chofunikira kwambiri kwa amene ali ndi chikhumbokhumbo chogwilira ntchito mu tchalitchi. Dag Heward-Mills, mu kalembedwe kake ka nthawi zonse, akupeleka malamulo ogwilira mu utumiki wa nthawi zonse komanso kubweletsa bvumbulutso lofunikira kwambiri pa kuchita bwino mu utumiki. -
Bukhu limeneri ndi chotsatira chomwe chadikiridwa kwambiri cha “M’busa Wamba ndi Utumiki”. Kumaimira kusiyana kwa pakati pa utumiki wa munthu wamba ndi utumiki wa nthawi zonse. Mu bukhu lapaderali Dag Heward-Mills akukulimbikitsani kuti mukadzipereke nokha kwa thunthu kwa Mulungu ndi kukupangitsani kupeza zifukwa zoyenera zolowera mu utumiki wa nthawi zonse. -
Chilichonse chimene Mulungu amanena chimafuna kuleza mtima ndi "Mau a chipiriro changa". Ambiri mwa malonjezano a Mulungu ndi zitsanzo za "Mau a chipiriro changa". Mulungu amalonjeza zinthu zambiri m’Baibulo, koma ambiri mwa malonjezo amenewa amafuna chipiriro kuti akakwaniritsidwe. Kachikenanso, Bishopu Dag Heward-Mills, akufotokoza mosamalitsa m’bukhuli, zokumana nazo za amuna aakulu a m’Baibulo amene anafunika kupirira “Mau a chipiriro changa” kuti akalandire malonjezo a Mulungu. -
Mfundo ndi chivumbulutso! Mfundo ndi chinachake chimene chimakulola kuti ukule! Mfundo ndi kumvetsa mozama mmene chinthu chimagwirira ntchito. Bukuli lili ndi mfundo zosiyanasiyana, zonse zokhudzana ndi chipulumutso chachikulu chimene takumana nacho mwa Khristu! Lolowerani mozama pa kumvetsa kwanu chipulumutso pamene mukuphunzira mfundo zazikulu zisanu ndi ziwiri izi. Pamene mukuchita zimenezi, Mulungu adzaika m'manja mwanu makiyi amene adzakutsimikizirani kukwera m’magulu apamwamba kwambiri mwa Iye. -
Mutalandira Yesu Khristu ngati Mbuye ndi Mpulumutsi wanu mumapulumutsidwa! Inu ndinu Mkhristu wobadwanso mwatsopano ndipo dzina lanu lalembedwa mu Bukhu la Moyo. Funso lanu ndilo: "Kodi sitepe yotsatira ndi yotani?" Pokhala Mkhristu ndi sitepe yabwino, koma ndi chiyambi chabe. Inu mukuyenera kukhala Mkhristu wabwino, wamphamvu. 'Nanga ndichita bwanji izi?' - M'buku ili labwino, mudzaphunzira njira zoti mutenge ndikukhala Mkhristu wamphamvu yemwe ali wokonzeka kufa kapena mkwatulo. -
Dr. Dag Heward-Mills, mtsogoleri wa Chikhristu wopambana, akuonetsa chimodzi mwa zinsinsi zake. “Ngati wina atandifunsa chomwe chinsinsi changa chachikulu cha ubale wanga ndi Mulungu chiri, nditha kunena, musaopa, kuti ndi mphamvu ya nthawi za chete yomwe ndimakhala nayo ndi Iye tsiku ndi tsiku.” Iwe waganiza kulemba bukhuli kuti inunso mukapindule kuchokera ku mphamvu ya nthawi ya chete. -
“Ndingapemphere bwanji? Kodi ndipempherere chani? Kodi pemphero ndilodabwitsa chifukwa chani? Ndingapemphere bwanji kwa nthawi yaitali? Kodi Mulungu sakudziwa zomwe ndikufuna? Mapemphero anga ayankhidwadi?” Pezani mayankho a mafunso amenewa pomwe mukuwerenga bukhu lobwera panthawi yake lolembedwa ndi Dag Heward-Mills.