Dag Heward-Mills ndi wolemba wa mabuku ambiri, kuphatikizapo logulitsidwa kwambiri “Kukhulupirika ndi Kusakhulupirika”. Ndi woyambitsa wa Mipingo ingapo yochokera ku Lighthose ndi matchalitchi zikwi zitatu.
Dag Heward-Mills, mvangeli wadziko lonse, amatumikira mu misonkhano ya machiritso mu maiko komanso misonkhano ya atsogoleri padziko lonse. Kuti mudziwe zambiri, pitani pa
www.daghewardmills.org.

  • Nthawi zambiri timalimbikitsika pamene tikamaganizira za mfundo yoti “Ambiri Aitanidwa”. Kenako tonse mwachangu timalimbikitsika tikamalingalira za mfundo yoti “…ochepa amasankhidwa.” Mutha kuwerengedwa ndi ambiri amene aitanidwa ndi ochepa amene asankhidwa ngati mupange bukhuli kukhala gawo la moyo wanu.Mu bukhu lodabwitsali lolembedwa ndi Dag Heward-Mills, muzazindikira kuchokera mu Baibulo zifukwa zomwe munganenere motsimikiza kuti ndinu oitanidwa. Inu mudzadziwa za makhalidwe a anthu oitanidwa ndipo muzalimbikitsidwa kukhala wosatekeseka mpaka kumapeto kwa ulendo wanu wa Chikhristu.
  • N’chifukwa chiyani Mulungu Wamphamvuzonse angafunike munthu? Kodi Ambuye angafunike chiyani kwa iwe? Kodi ndi chiyani chimene Mulungu sangathe kuchita yekha? Kodi ndi chiyani chimene Mulungu sangathe kukwaniritsa yekha? Mulungu akufunafuna munthu amene adzayime pakati pa Iyeyo ndi munthu. Mulungu akufunafuna munthu amene adzayankhe mafunso a ana ang’onoang’ono! Mulungu akufunafuna munthu amene adzafikire ana osatetezedwa! Baibulo limanena kuti Mulungu ankafunafuna munthu…!

    M’mene ukwerenga bukuli lonse, Warmth for the Heart, chikhumbo chako chokhala chombo chofunitsitsa kugwiritsidwa ntchito m’manja a Mulungu chidzaukiridwa. Sudzakhalanso wokhutira kungokhala membala wamba. Udzakhala munthu wothandiza! Udzanena ngati woimba wotchuka uja: “Ambuye, ndikudziwa kuti mukufunikira munthu! Mungandidalire ine!”

  • Anagkazo amatanthauza “kukakamiza”.Amatanthauzanso kupangitsa kuti chifunike, kukusira, ndi kupanikiza mwa njira iliyonse monga kuumiriza, kuwopseza, kukopa ndi kuchonderera. Nthawi zina tiyenera kubwerera ku Chigiriki kuti timvetsetse matanthauzo enieni la mawu ena a M'baibulo. Mukuona, Chipangano Chatsopano chinamasuliridwa kuchokera kuchilankhulo cha Chigiriki ndipo Chipangano Chakale kuchokera ku Chihebri. Anagkazo ndi liwu la Chigiriki lomwe limamasuliridwa kuti "kukakamiza".
  • Minda yayera ndipo kholola la miyoyo lacha, koma alaliki ali kuti? Bukhu lolimbikitsa latsopano la Dag Heward-Mills ndi muitano wachangu kwa Akhristu kukhala otengera miyoyo kwa Khristu.
  • Mu bukhu lapamwambali, Dag Heward-Mills akupereka kuzindikira kwakukulu kwa zochitika m'banja. Bukhu lodabwitsali likagwira ntchito ngati chipangizo chokonzekera kwa phungu wa banja ndi anthu okwatira. Inu mukapeza mu bukhuli, mfundo zotsitsimutsa ndi zosangalatsa zopititsa patsogolo banja lanu. "Bukhu ili ndilodzadza ndi nkhani pa maziko ndi zochitika pa maubwenzi a umunthu mu nthawi imene musanakwatire, muli m'banja ndi ngakhale utatha ukwati. Ili ndi zipangizo zofufuzidwa bwino ndi zovomerezeka pa thunthu ndi kakhalidwe kazolengedwa pazogonana, kubereka kwa anthu, mimba ndi nthawi yobereka ikadutsa. Kuthekera kwa Dotolo Dag Heward-Mills kusintha nkhani zovuta kukhala zophweka ndiye chikhalidwe chosiyanitsa pa bukhuli. Zonse pamodzi, izi zimalipangitsa kukhala bukhu losindikizika lomveka kwambiri, logwiritsika ntchito bwino pa zabanja lero." David Asomani, katswiri wowona za chiberekero cha azimayi. "Bukhu la Bishopu Dag Heward-Mills pa uphungu wa m'banja ndilosowa chifanizo. Maziko ake ngati dotolo wa zachipatala zawonetsedwa momveka bwino mu tsatanetsatane, koma kudzifotokozera kwa zizindikiro zachipatala zomwe zikupangitsa bukhuli kukhala lapadera." Edwin Morgan Ogoe, Mphunzitsi, Sukulu Yaukachenjede ya Ghana, Sukulu Yazachipatala
     
  • M’bukuli lozama komanso lodzaza ndi nzeru, Dag Heward-Mills akufotokoza zimene zidzachitike pa BEMA – mpando woweruzira wa Khristu. Ngakhale kuti machimo athu akhululukidwa, pali chiweruzo chimene chikudikira okhulupirira onse. Chiweruzo chimatengera zimene wachita, zimene zabisika komanso zolinga za zochita zako. Zosankha ndizofunika kwambiri m’moyo. Kusowa kwa chiweruzo kumatanthauza kusowa kwa zosankha! Kusowa kwa chiweruzo kumatsogolera ku chipwirikiti! Luntha la wolemba pakuyankha mafunso ngati, “Kodi chiweruzo ndi chiyani?”, “N’chifukwa chiyani pali chiweruzo?”, komanso chifukwa chake Mulungu amakonda chiweruzo, lidzakutsogolerani kuzindikira kuti chiweruzo ndi chilungamo ndi zinthu zimene ziyenera kuphunzitsidwa, kumveketsedwa ndi kuphunziridwa kuti munthu akhale wokonzeka pa Tsiku la Chiweruzo!
  • Katundu wa Duma. Wina aitana kwa ine kucokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.Yesaya 21:11-12
  • Ambiri ayitanidwa, koma osankhidwa ndi ochepa. (Mateyo 22:14) Ndi choonadi cha moyo kuti anthu ambiri amapatsidwa mwayi waukulu, koma ndi ochepa amene amapindula mokwanira ndi mwayi umenewo. M’Baibulo lonse timaona chitsanzo cha anthu ambiri oyitanidwa koma potsiriza ochepa okha ndi amene amasankhidwa. N’chifukwa chiyani ochepa okha ndi amene amasankhidwa? Funso lakuti n’chifukwa chiyani ochepa okha amasankhidwa ndilo funso lalikulu limene tikufuna kuyankha m’bukuli. Mutatha kuwerenga bukuli losankhidwa bwino lolembedwa ndi wolemba wotchuka Dag Heward-Mills, mudzazindikira mmene zimakhalira kuti anthu ambiri ayitanidwe koma ochepa asankhidwe. Ndikupemphera kuti musatengere mopepuka kuitanidwa kumeneku, komanso mugwire ntchito molimbika kuti mukhale m’modzi mwa ochepa amene amasankhidwa!
  • Anthu ambiri amavutika ndi lingaliro la kupereka chakhumi ingakhale mchitidwe wakale kalewu wabweretsa chuma kwa Ayuda. Mu bukhuli, Bishopu Dag Heward-Mills akuphunzitsa momwe kupereka chakhumi kumapezera mfundo zikulu zikulu za kupanga chuma ndi zozwizitsa za kuchita bwino. Sangalalani ndi limodzi mwa makope a Dag Heward-Mills.
  • Ngati Mkhristu, chikoka chachikulu komanso chokometsetsa mu moyo wanu chikuyenera kukhala Mzimu Woyera. Bukhuli likukulolani kumvetsetsa khalidwe lanu, kuzindikira kwanu, luso lanu ndinso kuthekera kwanu kokhala woyera kutha kukokedwa ndi Mzimu Woyera. Kudzera mu bukhu lapamwambali lolembedwa ndi Dag Heward-Mills, mukuyenera kulola Mzimu Woyera kukukokani, kukulimbikitsani, kukukhadzani komanso kusintha moyo wanu kwa muyaya.
  • Mulungu akufuna kuti anthu onse apulumutsidwe! N'chifukwa chake anatuma Yesu Khristu kuti adzatifere. Yesu adagwiritsa ntchito magazi ake kulipira machimo athu. Ife omwe tapulumutsidwa, Mulungu akutitana kuti tikhale opulumutsa a anthu. Twapatsidwa Lamulo Lalikulu Lotumiza. Mawu omaliza a Yesu kwa ife ndi awa: tipite kudziko lonse lapansi, tikapange ophunzira mwa anthu onse! Kodi udzayankha kuitanidwa kumeneku? Ili ndi mutu wina woyanitsa maganizo m'mndandanda wachikhalidwe wa mabuku a mauthenga a chipulumutso olembedwa ndi Dag Heward-Mills. Mosakayikira, buku ili lidzalimbikitsa wokhulupira aliyense kukwaniritsa udindo wake kwa ochimwa ndi kukhala wopulumutsa wa anthu!
  • Pamene muyenda mmoyo inu mukapeza kuti dziko lobisika ndi dziko lenileni ndipo dziko lakuthupi ndi chiwonetsero cha zina mwa zinthu zamu dziko lobisika. Monga mmene mulili ndi adani owoneka, inu mulinso ndi adani obisika. Kodi mungamenyane ndi mdani osamudziwa iye, ndondomeko zake, kapangidwe kake ka zinthu ndi zida zake? Bukhu ili ndi chida chofunika ku ulendo wa moyo wanu. M'bukhu ili mukaphunzira kuti adani anu obisika ndi ati, mizu yakukhala kwawo, maonekedwe awo ndi momwe mungapambanire nkhondo ndi iwo. Bukhu labwinoli likuthandizeni kugonjetsa adani anu obisika!
     
  • Baibulo limatilangiza ife ku: "Munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzakeyo" (Afilipi 2:4). M'bukhu la m'nthawi yakeli, Dag Heward-Mills akukuwuzani inu mupitirire kuganiza za inu nokha ndi kuganizanso za ena! Mukondenso ena! Muganizirenso ena! Musamalenso za ena! Mukhalenso chifukwa cha ena! Yesu anadza kudzatifera ife chifukwa Iye anaganiza za "ena". Ine ndikufuna kukhala kwambiri ngati Iye. Kodi inu mukufuna kukhala ngati Yesu?
  • Anthu ambiri amapereka maola ambiri akugwira ntchito ndi cholinga chimodzi chokha – kukhala olemera! Tsoka ilo, chuma chimawatha m'manja anthu ambiri pamene amalifuna molimbika kukhala olemera. Chifukwa chiyani? Chifukwa amafuna kungokhala olemera, pamene pali cholinga chapamwamba, choposa chuma, chimene Mulungu amafuna kuti uzigwirira ntchito. Bukuli likufotokoza zinthu zimene Baibulo limanena kuti uyenera kupereka moyo wako kuzochita zimenezo. M’malo mongogwira ntchito kuti ukhale wolemera, udzaphunzira kugwira ntchito chifukwa cha zinthu zapamwamba! Landirani masomphenya atsopano okhala dalitso kwa ena pamene mukuwerenga bukuli latsopano, lokopa chidwi, lolembedwa ndi Dag Heward-Mills!
  • Baibulo limatichenjeza mosapita m’mbali kuti zokhumudwitsa zidzafika kwa ife.  Izi zikutanthauza kuti padzakhala zochitika m'moyo chomwe sichingakusangalaseni ndikukukhumudwitsani. Kodi chenjezo limeneli limatikonzekeretsa mokwanira kuti tigonjetse pamene takhumudwitsidwa?  Kodi mungadzitetezere kuti musakhumudwe? Kodi mudzalola kuti kukhumudwitsa kukupangitseni kusakhulupirika chinthu chamtengo wapatali chotchedwa “kudalira”?  Bukhuli ndi bukhu lanu la mayankho ku mafunso owopsa awa. M’bukhu ili, Dag Heward-Mills akufotokoza zotsatira za zolakwa pa ife. Timaphunzira kuti zolakwa zimatipweteka ndi kutikwiyitsa, komanso kuti zolakwa zina zimakhala zovuta kuzikhululukira ndi kuziiwala. Bukhulinso ndi chida chophunzirira momwe tingagonjetsere zolakwa kuti tisakhale akapolo a kukhumudwa.
  • Mu bukhu lapamwambali, Bishop Dag Heward-mills amaphunzitsa za momwe chida cha kukhulupirika chimalimbikitsa kachitidwe ka mtsogoleri. Kugwiritsa ntchito baibulo, mbiri ndi zolemba, mutu uwu wapangidwa kukhala woyenera kwa wowerenga.
  • Bukhu iri ndi mphatso ina kuchokera ku cholembera cha Dag Heward-Mills kwa azitumiki onse amene atha kupeza nthawi yowerenga. Bukhuli lizayankha mafunso onse okhuzana ndi momwe mungakwaniritsire kukhala ndi ubale wabwino pakati pa atate ndi ana. Kudzera mu chiphunzitso cha bukhu limeneri, muzapewa themberero pa moyo wanu ndi kubweretsa kwanokha mdalitso. Atate ndi anthu apadera amene amakuza ana. Popanda atate sipazakhala ana kupitiriza utumiki ku mibadwo ina. Maitanidwe a Mulungu amakula kapena kufa ndi kuthekera kochitirana ndi atate. Werengani bukhu limeneri ndipo pewani themberero lokhuzana ndi kusalemekeza, kusamvera ndi kukhala ndi ubale woipa ndi atate.
  • Kudzikweza ndi poizoni wakupha amene waononga mtundu wa anthu mzaka zambiri. Chifukwa nkosatheka, kudzikweza kumakwaniritsa kupangitsa chionongeko chachikulu popanda kuonekera. Tingamenyane bwanji ndi chiopsezo chimenechi ku miyoyo yathu? Ndi katemera wa kudzichepetsa! Kudzichepetsa ndi chabwino chauzimu. Ochepa akwanitsa kulemba zokhudzana ndi chofunikira chauzimuchi. Mu bukhu latsopano losangalatsali, Dag Heward-Mills akuonetsera mitundi yobisika ya kudzikweza. Bukhu la mphamvu limeneri, lolembedwa ndi Mkhristu wovutika mzathu, likudalitsani ndi kukulimbikitsani inu kukuza kudzichepetsa konga mwana kwa Yesu Khristu.
  • Anthu opanduka samakumbukira zomwe zapangidwa kwa iwo ndipo nthawi zambiri amasankha kuiwala zinthu zina. Yudase sanakumbukire zimene Ambuye anamchitira, ndinso sanakumbukirenso zinthu zimene anaona ndi kumva kwa Yesu. Ichi ndi chifukwa chake adakhala mtundu wa munthu amene tikumudziwa lero ngati ‘Yudase’. Kuthekera kokumbukira ndi chimodzi mwa zinthu zauzimu chomwe mtumiki atha kukhala nacho. Anthu amene samakumbukira, siwamba kuchita bwino. Iwo amalephera kufika mlingo wina. Bukhu lapaderali, pa mutu wosakambidwa kwambiriwu ndi mphamvu yochokera kwa Mulungu kwa inu.
  • Ulemu ndi chinthu chofunika kwambiri chimene aliyense ayenera kuchidziwa. Kupereka ulemu ndi lamulo la m’Baibulo. Ulemu ndi wofunika kwambiri mu ubale wako ndi Mulungu. Ulemu ndi wofunika kwambiri mu ubale wako ndi mneneri wako, abusa ako, mwamuna wako ndi ena onse amene ali ndi udindo pa iwe. Ukasapatsa ulemu kwa amene ulemu wake uyenera kuperekedwa, sudzakhala ndi ubale woyenera ndi anthu ena ena. Ili ndi buku la malangizo a moyo. M’bukuli mudzaphunzitsidwa mmene mungalemekezere munthu, zizindikiro za kusalemekeza, mphotho za ulemu ndi zina zambiri. Bukuli lili ndi makiyi okuthandizani kusunga ndi kuteteza maubale anu ofunika. Musapezeke osakwanira pankhani ya ulemu!
  • “Mwina mmodzi mwa adani aakulu omwe mutha kukumana nawo ndi ‘woneneza pakati pa abale’.” Landirani chidziwitso chachikulu cha momwe chida chimenechi cha kuneneza chimadzera ndipo phunzirani za momwe mungachigonjetsere, pomwe mukuwerenga bukhu lapamwambali, lolembedwa ndi Dag Heward-Mills.
  • Anthu amene amakusiya atha kukuwonongani. Palibe chimene chingalongosera kumva kwa kukhumudwa, kubalalika ndi nkhawa zimene zimadza pamene anthu akukusiyani. Bukhu ili lalembedwa kukuthandizani inu kulimbana ndi chiwonongeko chomwe chimadza pamene anthu akusiyani. Musanyengedwe. Kusiidwa sikwachilendo kwa inu ndi utumiki wanu. Ambiri ena avutika ndi zomwezo. Satana anali wopanduka woyamba ndipo akulimbikitsa opandukira onse kuyambira pamenepo. Ndi bukhu limeneri mu manja anu, muzachirimika ndi kulimbana ndi mzimu wa kusakhulupirika umene umadza ndi “iwo amene amakusiyani”.
  • Mipingo yadzadzidwa ndi onamizira angwiro amene amakhala osakhulupirika mwangwiro. Chida cheni cheni cha Satana chakhala chinyengo ndi kunamizira. Mtsogoleri amene sazindikira wonyenga azavutika chifukwa cha kusaona kwake.Kuopseza, chizolowezi ndi chisokonezo ndi mizimu yoipa imene imalimbana ndi azitumiki. Nthawi zambiri, anthu samadziwa chomwe chimalimbana nawo. Bukhu ili likakuthandizani inu kudziwa ndi kulimbana ndi mdani wamkati.
  • Yesu Khristu akuonetsera mfundo yodabwitsa yomwe ikutsogolera kuchita bwino ndi chuma. Iye amene ali nako kanthu azakhala nazo zambiri! Zikumveka mokondera! Koma, ichi ndi chilungamo chomwe chikuonetsedwa kwa ife tsiku ndi tsiku. Bukhuli likulongosola Lemba losamvetsetseka kwambiri iri. Muzalandira chidziwitso chachikulu ku zinsinsi za kuchita bwino pamene mukuwerenga bukhu latsopanoli lolembedwa ndi Dag Heward-Mills.
  • Kukhala wokhulupirika mpaka imfa ndiko kusagonjera moyo wako wonse! Kukhala wokhulupirika mpaka imfa ndiko kukhala wokhulupirika, wokhazikika, wofanana, wosagwedezeka ndi wosasintha kufikira imfa. Pamene mukupitiriza utumiki wanu kwa Ambuye, ndithudi mudzakumana ndi chochitika chopunthwa, kugwa, ndi kusakhulupirika.  Yesu akutichenjezanso ku Mateyu 18:7 kuti “…ziyenera kuti zokhumudwitsa zibwere; …” Anthu ambiri amathamanga ndi kufika pamalo pomwe amagwa mwadzidzidzi ndi kugwa pansi pazifukwa zina.  Zopunthwitsa zingapangitse kukhala kosatheka kufika mapeto omwe akuyembekezeredwa.   Izi ndi zomwe muyenera kupewa! Onetsetsani kuti musagwe pansi ndikutuluka mumpikisanowo. Izi ndi mfundo za Mpulumutsi wathu ndipo ndikofunikira kuti muziwakhulupirira ndikuzichita.  Bukhu lapanthawi yake ili lolembedwa ndi wolemba wotchuka Dag Heward-Mills, likulimbikitsani kukhalabe wokhulupirika mpaka kumapeto.
  • Aliyense amene sagwiritsa ntchito luso lake lopatsidwa ndi Mulungu pa ufumu, ndi wosabala zipatso ndipo ndi chifaniziro cha mchere umene wataya fungo lake.  Yesu anati, kapolo wopanda pake sapindula kanthu.  Kodi mulibe phindu mu ufumu?  Inu ndinu mchere wa dziko lapansi, kotero muyenera kumveketsa kukhalapo kwanu padziko lapansi lino! Bukhu ili launeneri ndi lopatsa kuganiza mozama za mchere ndi chikoka chake chachinsinsi ndi phindu launeneri ku ufumu wa Mulungu, lidzakupangitsani kulingalira mozama za ubwino wanu kapena kusowa kwake, kwa Mulungu.  Muphunzira m’bukhu lovutali tanthauzo la kukhala wopanda pake posanthula ndi kumvetsetsa udindo wa mchere m’miyoyo yathu. OSATI kukhala wabwino pachabe!
  • Lero pali zinthu zing’onozing’ono zambiri zimene tingachite zomwe zingabweretse kusiyana kwakukulu pa khama lonse lomangira ufumu wa Mulungu. Khama lochulukirapo pang’ono, nthawi yowonjezerapo pang’ono, ndalama zowonjezerapo pang’ono zoyendetsera patsogolo ntchito ya Khristu, chidwi chowonjezerapo pang’ono pa moyo wa munthu wosapulumutsidwa, chisamaliro chowonjezerapo pang’ono kwa mnansi wako — zonsezi zingabweretse kusiyana kwakukulu. Kodi sungathe kungachita zowonjezerapo pang’ono chabe? Uwu ndi kuyitanidwa kwamphamvu komveka bwino komwe sitinganyalanyaze! Kodi sungathe kungachita zowonjezerapo pang’ono chabe?
  • Cholinga chamuyaya cha Mulungu kwa ife ndikuti tikhale obala zipatso. Mu Yohane 15:16, Ambuye Yesu analangiza ophunzira ake kuti “pitani mukabale zipatso” Mulungu amakuonani inu ngati mtengo umene uyenera kubala zipatso. Mu bukhu lothandiza ili, Bishopu Dag Heward-Mills akutitengera ife kupyola mu Malamulo a Kubala Zipatso osiyanasiyana a m'baibulo otengedwa m'Baibulo. Mudzalimbikitsidwa kubala zipatso zambiri - chipatso chomwe chidzakhala!
  • Ngakhale ndi mutu wachilendo, kubwerera m’mbuyo kumachitirana ndi zopezeka mwa wamba mwa Akhristu. Ambiri amayamba, koma si ambiri amene amapirira. Mu bukhuli, Bishopu Dag Heward Mils akuchenjeza, ndi kuwonetsa zifukwa zomwe Mkhristu aliyense akuyenera kukafikira Kumwamba!
  • Kubzala mipingo ndi chinthu chomwe chafalikira pakati pa azitumiki a uthenga wabwino. Inali ntchito ya ophunzira oyambirira. Kubzala mipingo kopambana kumafuna luso ndi zina zambiri. Dag Heward-Mills, woyambitsa matchalitchi zikwi zitatu padziko lonse, akutitsogolera ife kuunikira zinthu zosiyana siyana za kubzala mpingo mu bukhuli. Ili ndi kope la kuphunzirirapo kwa mtumiki ali yense amene akufuna kupanga kubzala mipingo kukhala masomphenya ake a moyo ndi utumiki.
  • Kukhalapo kwa Mulungu n’kwamtengo wapatali! Kukhalapo kwa Mulungu n’kofunika! Kukhalapo kwa Mulungu n’kofunika kwambiri pa miyoyo yathu, ndipo tiyenera kulikufuna ndi mitima yathu yonse. Sititha konse, m’njira iliyonse, kuchepetsa kufunika kwa kukhalapo kwa Mulungu pa kuyenda kwathu naye. Tiyenera nthawi zonse kukhala tikulifunafuna kukhalapo kwa Mulungu. Kukhala ndi kukhalapo kodzozedwa pamodzi nanu, n’kukhala ndi Kukhalapo Kopatulika kwa Mulungu m’moyo mwanu. Ndi pemphero langa kuti mtima wanu utsitsimuke kulakalaka kukhalapo kwa Mulungu kwamtengo wapatali pamene mukuwelenga buku lodabwitsali lolemba Dag Heward-Mills.
  • "Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, khululukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhululukire inu zolakwa zanu. Koma NGATI INU SIMUKHULULUKIRA, ATATE WANU WAKUMWAMBA SAZAKHULULUKIRA INU ZOLAKWA ZANU" (Marko 11:25-26). Kodi ndimezi zikukunjenjemeretsani? Yankho lanu lilipano. Mu bukhu lofunikirali, muphunzira kukhululukira mosavuta - kutinso nanu musangalale ndi chikhululukiro cha Atate wanu wakumwamba. Mulole kuti bukhu ili likhale bwenzi lanu mpaka mutafika poti mukutha kukhululukira mosavuta ndi moona mtima.
  • Ingakhale ndi chofunikira choyamba cha Mulungu kwa atsogoleri, zochepa kwambiri zalembedwa pa mutu uwu. Mu bukhuli, Dag Heward-Mills akutchula mfundo zikulu zikulu ndi cholinga chokulitsira kukhadzikika kwa matchalitchi. Zamkati mwa bukhuli zili zoyenerera komanso zochitika mpaka ndi kukhala chida chosasiidwa kwa atsogoleri ambiri.
  • Bukhu lija la abusa ndi akazi a abusa lafika! Bukhu ili silikhudza inu ngati sindinu mbusa kapena mkazi wa mbusa! Ngati inu muli oyenerezeka kuwerenga bukuli, muloleni Mulungu akutumikireni inu mu buku loshosha maganizoli. Mu masambawa, maudindo achinsinsi omwe akazi achita mu miyoyo ya azibusa awululika. Masambawa akulangizeni inu ndi kukudzetsani inu m'njira ya mdalisto!
  • M’Baibulo muli umboni woonekeratu wosonyeza kuti zinthu zimakonzedweratu.  Kukhulupirira choikidwiratu kumatanthauza kuti mumakhulupirira kuti palibe amene ali ndi ulamuliro weniweni wa zochitika koma kuti chirichonse chasankhidwa kale ndi dongosolo ndi chifuniro cha Mulungu.  Kumbali ina, palinso umboni wakuti Mulungu amatipatsa ufulu wosankha komanso kutilola kukhala ndi ufulu wosankha chabwino ndi choipa. Lingaliro la choikidwiratu n’lovuta kulimvetsa chifukwa cha mmene zinthu zimachitikira.   Koma kukonzedweratu ndi koonadi!  Yakwana nthawi yoti mumvetsetse kukonzedweratu kuti muthe kugwira ntchito ndi Mulungu ndi kuyenda ndi Mulungu mosavuta. Nkhani ina yochititsa chidwi yolembedwa ndi wolemba wotchuka, Dag Heward-Mills. Khulupirirani Mulungu ndikuwona kuwonekera kwa zinthu zonse zomwe Mulungu wakukonzerani inu.  

Title

Go to Top